26.5 C
Blantyre
Thursday, June 1, 2023

Alodza Mwana Wake Kuti Asazakwatiwe Kamba Ka Umbombo

Must read

Mtsikana wina yemwe amagwila ntchito ya uphunzitsi pa sukulu ina ku Dwangwa m’boma la Nkhotakota akulila usiku ndi usana mai ake omubala atamuthetsela banja.

Nkhani-yi ikuti mtsikana-yo atayamba ntchito anaganiza zokwatiwa koma amuna samamufunsila.

Kenaka panamveka mphekesela yoti mai ake anamuchitila mankhwala kuti asakwatiwe ati poganiza kuti zonse zomwe amawachitila mai ake-wo asiya.

Apa mtsikana-yo akuti naye anaganiza zopondaponda ndipo anapeza mtela omwe unakwanitsa kumumasula ku msinga za mai ake-wo.

Ndipo posakhalitsa mtsikana-yo anapeza banja.  Awiri-wa akuti anagwilizana kuti adzikhala mnyumba yomwe mtsikana-yo anamanga kwao.

Koma mmalo mokondwa mai wa mtsikana-yo  kuti anayamba kupezela zifukwa mwamuna-yo ponena kuti ndi mphawi.

Koma ngakhale mtsikana-yo anayesetsa kuikila kumbuyo mwamuna wake mkutemetsa nkhwangwa pa mwala kuti sasiyana ndi mwamuna-yo naye mai-yo anachita chotheka mpaka kuthetsa banja-lo.

Mtsikana-yo akuti anadandaula kwambiri ndi zomwe mai ake anachita.   Koma patangotha miezi yochepa mtsikana-yo akuti anakwatiwanso ndi mkulu wina.   Mai wa mtsikana-yo mmalo mokondwa kuti mwamuna wa tsopano-yo yemwe anali wamakobili ake  akuti anapitiliza kuvutitsa mwana wake kuti athetse banja-lo.

Mai-yo akuti anayamba kumalalatila mpongozi-yo pa maso ndipo mpongozi-yo atatopa ndi khalidwe-li anathetsa banja-lo.   Pakadali pano mtsikana-yo akuti akukhala khuma kamba ka zomwe mai ake amuchita.

- Advertisement -spot_img

More articles

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -spot_img

Latest article