Mkulu wina kwa Wimbe mboma la Kasungu wazunguzia mutu munthu wina yemwe sakudziwika atagwira njoka yake yokawa.
Nkhaniyi ikuti mkuluyo ndi nkhalakale pa bizinesi koma zimamveka kuti ali ndi njoka yokawa.
Mwa zina anzake a bizinesi pa sitolozo akagulitsa katundu, ndalama sizimaoneka bwino ndipo atafufuza bwino anadziwa kuti mkuluyo akumakawa ndalama za anzake.
Ena mwa abizinesiwo akhala akumufunsa nkhaniyi komanso kumudandaulira kuti ngati nkhaniyi ili yoona asinthe khalidwelo, koma mkuluyo amakanitsitsa kwa ntu wa galu kuti sakudziwapo kanthu pa nkhani yokawayo.
Tsono masiku apitawa anzakewo atatopa nkugwira ntchito ya bule, anamupita pansi kumupitilira kwa sing’anga wina kukatenga mankhwala woti njoka yakeyo ikapita kokawako, ikakodwe komweko.
Dzana laliwisili, mkuluyo anatuma njoka yakeyo kupita ku golosake ya Chikhwaya china ndipo inakakodwa komweko. Mkuluyo anaswera usiku onse osagona kudikira njoka yakeyo koma ku njira kunali zii ndipo apa anangodziwiratu kuti yalakwa. Kutacha m’mawa mkuluyo anakhala ngati wapenga chifukwa amangofunsa aliyense za njoka yakeyo koma samatchula kuti njoka amangoti katundu wake wasowa. Mkuluyo anayenda pafupifupi dera lonselo koma palibe anamuyankha zomveka.
Mkuluyo panopa akusowa mtengo wogwira moti akungochondelera aliyense kuti ngati akumusungira katundu wakeyo angokambirana kuti alipire ndalama zingati kuti amupatse katundu wakeyo.
Pakadali pano anthu ambili m’deralo ati nkutheka kuti alipo yemwe akusunga katundu wa mkuluyo koma akungofuna kumukhaulitsa kuti asiye mchitidwe wake oipawo.